8 Kulibe munthu ali ndi mphamvu yolamulira mzimu ndi yakutsekereza mzimu; ngakhale mphamvu tsiku la imfa; munkhondo umo mulibe kumasuka; udio sudzapulumutsa akuzolowerana nao.
9 Zonsezi ndaziona ndi kuyang'anitsa mtima wanga nchito zonse zicitidwa pansi pano; nthawi yakuti wina apweteka mnzace pomlamulira.
10 Ndipo ndinaona oipa alikuikidwa m'manda ndi kupita; ndipo omwe anacita zolungama anacokera ku malo opatulika a ku mudzi nawaiwala; icinso ndi cabe.
11 Popeza sambwezera coipa cace posacedwa atamtsutsa munthu, ana a anthu atsimikizadi mitima yao kucita zoipa.
12 Angakhale wocimwa acita zoipa zambirimbiri, masiku ace ndi kucuruka, koma ndidziwitsadi kuti omwe aopa Mulungu naopa pamaso pace adzapeza bwino;
13 koma woipa sadzapeza bwino ngakhale kutanimphitsa masiku ace ngati mthunzi; cifukwa saopa pamaso pa Mulungu.
14 Pali cinthu cacabe cimacitidwa pansi pano; cakuti alipo olungama amene aona zomwe ziyenera nchito za oipa, ndipo alipo oipa amene aona zomwe ziyenera nchito za olungama, Ndinati, Icinso ndi cabe.