1 Ndipo ndinakwezanso maso anga, ndinapenya, ndipo taonani, anaturuka magareta anai pakati pa mapiri awiri; ndi mapiriwo ndiwo mapiri amkuwa.
2 Ku gareta woyamba kunali akavalo ofiira; ndi ku gareta waciwiri akavalo akuda;
3 ndi ku gareta wacitatu akavalo oyera; ndi ku gareta wacinai akavalo olimba amawanga.
4 Ndipo ndinayankha ndinati kwa mthenga wolankhula ndi ine, Izi nziani, mbuyanga?
5 Ndi mthenga anayankha, nati kwa ine, Izi ndi mphepo zinai zakumwamba zakuturuka kumene zimaimirira pamaso pa Ambuye wa dziko lonse lapansi.
6 Gareta wa akavalo akuda aturukira ku dziko la kumpoto; ndi oyerawo aturukira kuwatsata; ndi amawanga aturukira ku dziko la kumwela.