18 Pamenepo anandikhudzanso wina, maonekedwe ace ngati munthu, nandilimbikitsa ine.
19 Nati, Munthu wokondedwatu iwe, Usaope, mtendere ukhale nawe; limbika, etu limbika. Ndipo pamene ananena ndi ine ndinalimbikitsidwa, ndinati, Anene mbuye wanga; pakuti mwandilimbikitsa.
20 Pamenepo anati, Kodi udziwa cifukwa coti ndakudzera? ndipo tsopano ndibwerera kulimbana ndi kalonga wa Perisiya; ndipo pomuka ine, taonani, adzadza kalonga wa Helene.
21 Koma ndidzakufotokozera colembedwa pa lemba la coonadi; ndipo palibe wina wakudzilimbikitsa pamodzi ndi ine, kutsutsana ndi aja, koma Mikaeli kalonga wanu.