14 Anapfuulitsa, natero, Likhani mtengowo, sadzani nthambi zace, yoyolani masamba ace, mwazani zipatso zace, nyama zicoke pansi pace, ndi mbalame pa nthambi zace.
15 Koma siyani citsa ndi mizu yace m'nthaka, comangidwa ndi mkombero wa citsulo ndi mkuwa, mu msipu wa kuthengo; ncokhathamira ndi mame a kumwamba, ndi gawo lace likhale pamodzi ndi nyama ziri m'macire a m'dziko.
16 Mtima wace usandulike, usakhalenso mtima wa munthu, apatsidwe mtima wonga wa nyama, nizimpitire nthawi zisanu ndi ziwiri.
17 Citsutso ici adacilamulira amithenga oyerawo, anacifunsa, nacinena, kuti amoyo adziwe kuti Wam'mwambamwamba alamulira m'ufumu wa anthu, naupereka kwa ali yense Iye afuna, nauutsira wolubukira anthu.
18 Loto ili ndinaliona ine mfumu Nebukadinezara; ndipo iwe, Belitsazara, undifotokozere kumasulira kwace, popeza anzeru onse a m'ufumu wanga sakhoza kundidziwitsa kumasulira kwace; koma iwe ukhoza, popeza mwa iwe muli mzimu wa milungu yoyera.
19 Pamenepo Danieli, dzina lace ndiye Belitsazara anadabwa nthawi, namsautsa maganizo ace. Mfumu inayankha, niti, Belitsazara, lisakusautse lotoli, kapena kumasulira kwace. Belitsazara anayankha, nati, Mbuye wanga, lotoli likadakhala la iwo akudana nanu, ndi kumasulira kwace kwa iwo akuutsana nanu.
20 Mtengo mudauona umene unakula, nukhala wolimba, nufikira kumwamba msinkhu wace, nuonekera pa dziko lonse lapansi,