Danieli 4:17-23 BL92

17 Citsutso ici adacilamulira amithenga oyerawo, anacifunsa, nacinena, kuti amoyo adziwe kuti Wam'mwambamwamba alamulira m'ufumu wa anthu, naupereka kwa ali yense Iye afuna, nauutsira wolubukira anthu.

18 Loto ili ndinaliona ine mfumu Nebukadinezara; ndipo iwe, Belitsazara, undifotokozere kumasulira kwace, popeza anzeru onse a m'ufumu wanga sakhoza kundidziwitsa kumasulira kwace; koma iwe ukhoza, popeza mwa iwe muli mzimu wa milungu yoyera.

19 Pamenepo Danieli, dzina lace ndiye Belitsazara anadabwa nthawi, namsautsa maganizo ace. Mfumu inayankha, niti, Belitsazara, lisakusautse lotoli, kapena kumasulira kwace. Belitsazara anayankha, nati, Mbuye wanga, lotoli likadakhala la iwo akudana nanu, ndi kumasulira kwace kwa iwo akuutsana nanu.

20 Mtengo mudauona umene unakula, nukhala wolimba, nufikira kumwamba msinkhu wace, nuonekera pa dziko lonse lapansi,

21 umene masamba ace anali okoma, ndi zipatso zace zocuruka, ndi m'menemo munali cakudya cofikira onse, umene nyama za kuthengo zinakhala pansi pace, ndi mbalame za m'mlengalenga zinapeza pokhala pao pa nthambi yace;

22 ndinu, mfumu; mwakula, mwalimba, pakuti ukulu wanu wakula, nufikira kumwamba, ndi ufumu wanu ku cilekezero ca dziko lapansi.

23 Tsono, kuti mfumu inaona mthenga woyera wotsika kumwamba, ndi kuti, Likhani mtengowo ndi kuuononga, koma siyani citsa cace ndi mizu m'nthaka, comangidwa ndi mkombero wa citsulo ndi mkuwa, mu msipu wa kuthengo, nicikhale cokhathamira ndi mame a kumwamba, ndi gawo lace likhale pamodzi ndi nyama za kuthengo, mpaka zitampitira nthawi zisanu ndi ziwiri;