Danieli 4:31-37 BL92

31 Akali m'kamwa mwa mfumu mau awa, anamgwera mau ocokera kumwamba, ndi kuti, Mfumu Nebukadinezara, anena kwa iwe: ufumu wakucokera.

32 Nadzakuinga kukucotsa kwa anthu, ndi pokhala pako udzakhala pamodzi ndi nyama za kuthengo; adzakudyetsa udzu ngati ng'ombe; nizidzakupitira nthawi zisanu ndi ziwiri, mpaka udzadziwa kuti Wam'mwambamwamba alamulira m'ufumu wa anthu, naupereka kwa ali yense Iye afuna mwini.

33 Nthawi yomweyo anacitika mau awa kwa Nebukadinezara; anamuinga kumcotsa kwa anthu; nadya udzu ngati ng'ombe iye, ndi thupi lace linakhathamira ndi mame a kumwamba, mpaka tsitsi lace lidamera ngati nthenga za ciombankhanga ndi makadabo ace ngati makadabo a mbalame.

34 Atatha masiku awa tsono, ine Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndi nzeru zanga zinandibwerera; ndipo ndinalemekeza Wam'mwambamwamba, ndi kumyamika ndi kumcitira ulemu Iye wokhala cikhalire; pakuti kulamulira kwace ndiko kulamulira kosatha, ndi ufumu wace ku mibadwo mibadwo;

35 ndi okhala pa dziko lapansi onse ayesedwa acabe; ndipo Iye acita mwa cifunito cace m'khamu la kumwamba ndi mwa okhala pa dziko lapansi; ndipo palibe woletsa dzanja lace, kapena wakunena naye, Mucitanji?

36 Nthawi yomweyi nzeru zanga zinandibwerera, ndi cifumu canga ndi kunyezimira kwanga zinandibwerera, kuti uonekenso ulemerero wa ufumu wanga; ndi mandoda anga ndi akuru anga anandifuna; ndipo ndinakhazikika m'ufumu wanga, Iye nandioniezeranso ukulu wocuruka.

37 Tsono ine Nebukadinezara ndiyamika, ndi kukuza, ndi kulemekeza Mfumu ya Kumwamba, pakuti nchito zace zonse nzoona, ndi njira zace ciweruzo; ndi oyenda m'kudzikuza kwao, Iye akhoza kuwacepetsa.