7 Ndipo ndinamuona wayandikira pafupi pa nkhosa yamphongo, nawawidwa mtima nayo, naigunda nkhosa yamphongo, natyola nyanga zace ziwiri; ndipo mphongoyo inalibe mphamvu yakuima pamaso pace, koma anaigwetsa pansi, naipondereza; ndipo panalibe wakupulumutsa mphongoyo m'dzanja lace.
8 Ndipo tondeyo anadzikulitsa kwakukuru, koma atakhala wamphamvu, nyanga yace yaikuru inatyoka; ndi m'malo mwace munaphuka nyanga zinai zooneka bwino, zoloza ku mphepo zinai za mlengalenga.
9 Ndipo mu imodzi ra izi munaphuka nyanga yaing'ono, imene inakula kwakukuru ndithu, kuloza kumwela, ndi kum'mawa, ndi ku dziko lokometsetsa.
10 Nikula, kufikira khamu la kuthambo; ndi zina za khamulo ndi za nyenyezi inazigwetsa pansi, nizipondereza.
11 Inde inadzikulitsa kufikira kwa kalonga wa khamulo, nimcotsera nsembe yopsereza yacikhalire; ndi pokhala malo ace opatulika panagwetsedwa.
12 Ndipo khamulo linaperekedwa kwa iyo, pamodzi ndi nsembe yopsereza yacikhalire mwa kulakwa kwace, nigwetsa pansi coonadi, nicita cifuniro cace, nikuzika.
13 Pamenepo ndinamva wina woyera, alikunena; ndi wina woyera anati kwa iye uja wanenayo, Masomphenya a nsembe yopsereza yacikhalire, ndi colakwa cakupululutsa ca kupereka malo opatulika ndi khamulo ziponderezedwe, adzakhala mpaka liti?