3 Ninena naye mfumu, Mufunanji, Estere mkazi wamkuru? pempho lanu nciani? lidzaperekedwa kwa inu, kufikira limodzi la magawo awiri a ufumuwo.
4 Ndipo Estere anati, Cikakomera mfumu, adze mfumu ndi Hamani lero ku madyerero ndinawakonzera.
5 Niti mfumu, Mumfulumize Hamani, acitike mau a Estere. Nidza mfumu ndi Hamani ku madyerero adawakonzera Estere.
6 Ndipo mfumu inati kwa Estere pa madyerero a vinyo, Pempho lanu nciani? lidzaperekedwa kwa inu; mufunanji? cidzacitika, kufikira limodzi la magawo awiri a ufumuwo.
7 Nayankha Estere, nati, Pempho langa ndi kufuna kwanga ndiko,
8 ngati mfumu indikomera mtima, ngatinso cakomera mfumu kupereka pempho langa ndi kucita cofuna ine, adze mfumu ndi Hamani ku madyerero ndidzawakonzera; ndipo mawa ndidzacita monga yanena mfumu.
9 Ndipo Hamani anaturuka tsiku lomwelo wosekerera ndi wokondwera mtima; koma pamene Hamani anapenya Moredekai ku cipata ca mfumu, osamnyamukira kapena kumfumukira, Hamani anadzazidwa ndi mkwiyo pa Moredekai.