21 Ana a Aberi, a Hezekiya, makumi asanu ndi anai kudza asanu ndi atatu.
22 Ana a Hasumu, mazana atatu mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.
23 Ana a Bezai, mazana atatu mphambu makumi awiri kudza anai.
24 Ana a Harifi, zana limodzi mphambu khumi ndi awiri.
25 Ana a Gibeoni, makumi asanu ndi anai kudza asanu.
26 Amuna a ku Betelehemu ndi ku Netofa, zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu kudza asanu ndi atatu.
27 Amuna a ku Anatoti, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.