30 Amuna a ku Rama ndi Geba, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza mmodzi.
31 Amuna a ku Mikimasi, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.
32 Amuna a ku Betele ndi Ai, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza atatu.
33 Amuna a ku Nebo winayo, makumi asanu kudza awiri.
34 Ana a Elamu winayo, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri ndi makumi asanu kudza anai.
35 Ana a Harimu, mazana atatu mphambu makumi awiri.
36 Ana a Yeriko, mazana atatu mphambu makumi anai kudza asanu.