4 Atero Yehova Mulungu wanga: Dyetsani zoweta zakukaphedwa;
5 zimene eni ace azipha, nadziyesera osaparamula; ndi iwo akuwagulitsa akuti, Alemekezedwe Yehova, pakuti ine ndine wolemera; ndi abusa ao sazicitira cifundo.
6 Pakuti sindidzacitiranso cifundo okhala m'dzikomo, ati Yehova; koma taonani, ndidzapereka anthu, yense m'dzanja la mnansi wace, ndi m'dzanja la mfumu yace; ndipo iwo adzakantha dzikoli, ndi m'dzanja mwao sindidzawalanditsa.
7 M'mwemo ndinadyetsa zoweta zakukaphedwa, ndizo zoweta zonyankhalala. Ndipo ndinadzitengera ndodo ziwiri; yina ndinaicha Cisomo, inzace ndinaicha Comanganitsa; ndipo ndinadyetsa zowetazo.
8 Ndipo ndinatha abusa atatuwo mwezi umodzi; pakuti mtima wanga unalema nao, ndi mtima waonso unaipidwa nane.
9 Pamenepo ndinati, Sindidzadyetsanso inu; cirikufa cife; cosoweka cisoweke; ndi zotsala zidyane, conse nyama ya cinzace.
10 Ndipo ndinatenga ndodo yanga Cisomo, ndi kuidula pakati, kuti ndiphwanye pangano langa ndinalicita ndi mitundu yonse ya anthu.