3 ndi ku gareta wacitatu akavalo oyera; ndi ku gareta wacinai akavalo olimba amawanga.
4 Ndipo ndinayankha ndinati kwa mthenga wolankhula ndi ine, Izi nziani, mbuyanga?
5 Ndi mthenga anayankha, nati kwa ine, Izi ndi mphepo zinai zakumwamba zakuturuka kumene zimaimirira pamaso pa Ambuye wa dziko lonse lapansi.
6 Gareta wa akavalo akuda aturukira ku dziko la kumpoto; ndi oyerawo aturukira kuwatsata; ndi amawanga aturukira ku dziko la kumwela.
7 Ndi amphamvuwo anaturuka nayesa kumka kuyendayenda m'dziko; pakuti adati, Mukani, yendayendani m'dziko. Momwemo anayendayenda m'dziko.
8 Ndipo anandiitana, nanena nane, kuti, Taonani, iwo akuturuka kumka ku dziko la kumpoto anapumulitsa Mzimu wanga m'dziko lakumpoto.
9 Ndipo mau a Yehova anadza kwa ine, ndi kuti,