22 Mulungu wanga watuma mthenga wace, natseka pakamwa pa mikango; ndipo siinandipweteka, cifukwa anandiona wosacimwa pamaso pace, pamaso panunso, mfumu, sindinalakwa.
23 Pamenepo mfumu inakondwera kwambiri, niwauza aturutse Danieli m'dzenje. Momwemo anamturutsa Danieli m'dzenje, ndi pathupi pace sipadaoneka bala, popeza anakhulupirira Mulungu wace.
24 Ndipo italamulira mfumu, anabwera nao amuna aja adamneneza Danieli, nawaponya m'dzenje la mikango, iwowa, ana ao, ndi akazi ao; ndipo asanafike pansi pa dzenje mikango inawaposa mphamvu, niphwanya mafupa ao onse.
25 Pamenepo mfumu Dariyo analembera kwa anthu, mitundu ya anthu, ndi a manenedwe onse okhala pa dziko lonse lapansi, Mtendere ucurukire inu.
26 Ndilamulira ine kuti m'maiko onse a ufumu wanga anthu anjenjemere, naope pamaso pa Mulungu wa Danieli; pakuti Iye ndiye Mulungu wamoyo wakukhala cikhalire, ndi ufumu wace ngwosaonongeka, ndi kulamulira kwace kudzakhala mpaka cimariziro.
27 Iye apulumutsa, nalanditsa, nacita zizindikilo ndi zozizwa m'mwamba ndi pa dziko lapansi, ndiye amene anapulumutsa Danieli ku mphamvu ya mikango.
28 Momwemo Danieli amene anakuzikabe pokhala Dariyo mfumu, ndi pokhala mfumu Koresi wa ku Perisiya.