1 Caka cacitatu ca Belisazara mfumu masomphenya anandionekera kwa ine Danieli, atatha kundionekera oyamba aja.
2 Ndipo ndinaona m'masomphenya; tsono kunali, pakuwaona ine ndinali m'Susani, m'nyumba ya mfumu, ndiwo m'dziko la Elamu; ndinaona m'masomphenya kuti ndinali kumtsinje Ulai.
3 Ndipo ndinakweza maso anga ndi kupenya; taonani, panaima pamtsinje nkhosa yamphongo yokhala nazo nyanga ziwiri, ndi nyanga ziwirizo zinali za msinkhu wautali, koma imodzi inaposa inzace; yoposayo inaphuka m'mbuyo.
4 Ndinaona nkhosa yamphongo irikugunda kumadzulo, ndi kumpoto, ndi kumwela; ndipo panalibe zamoyo zokhoza kuima pamaso pace; panalibenso wakulanditsa m'dzanja lace; koma inacita monga mwa cifuniro cace, nidzikulitsa.
5 Ndipo polingirfrapo ine, taonani, wadza tonde wocokera kumadzulo, pa nkhope ya dziko lonse lapansi, wosakhudza nthaka; ndi mbuziyo inali ndi nyanga yooneka bwino pakati pa maso ace.
6 Ndipo anadzera nkhosa yamphongoyo yokhala ndi nyanga ziwiri, imene ndidaiona irikuima kumtsinje, naithamangira ndi mphamvu yace yaukali.
7 Ndipo ndinamuona wayandikira pafupi pa nkhosa yamphongo, nawawidwa mtima nayo, naigunda nkhosa yamphongo, natyola nyanga zace ziwiri; ndipo mphongoyo inalibe mphamvu yakuima pamaso pace, koma anaigwetsa pansi, naipondereza; ndipo panalibe wakupulumutsa mphongoyo m'dzanja lace.