23 Pakuti mfumu inalamulira za iwowa, naikira oyimbira cowathandiza, yense cace pa tsiku lace.
24 Ndi Petatiya mwana wa Mesezabele, wa ana a Zera, mwana wa Yuda, anatumikira mfumu pa mirandu yonse ya anthuwo.
25 Ndi ana ena a Yuda anakhala m'midzi ya ku minda yao, m'Kiriyati Ariba ndi miraga yace, ndi m'Diboni ndi miraga yace, ndi m'Yekabizeeli ndi midzi yace,
26 ndi m'Yesuwa, ndi m'Molada, ndi Betepeleti,
27 ndi m'Hazarisuala, ndi m'Beereseba ndi miraga yace,
28 ndi m'Zikilaga, ndi m'Mekona ndi miraga yace,
29 ndi m'Enirimoni, ndi m'Zora, ndi m'Yarimuti,