33 Amuna a ku Nebo winayo, makumi asanu kudza awiri.
34 Ana a Elamu winayo, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri ndi makumi asanu kudza anai.
35 Ana a Harimu, mazana atatu mphambu makumi awiri.
36 Ana a Yeriko, mazana atatu mphambu makumi anai kudza asanu.
37 Ana a Lodi, Hadidi, ndi Ono, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi awiri kudza mmodzi.
38 Ana a Senaa, zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi anai kudza makumi atatu.
39 Ansembe: ana a Yedaya, a nyumba ya Yesuwa, mazana asanu ndi anai mphambu makumi asanu ndi awiri kudza atatu.