1 Ndipo mau a Yehova wa makamui anadza kwa ine, ndi kuti,
2 Atero Yehova wa makamu: Ndimcitira nsanje Ziyoni ndi nsanje yaikuru, ndipo ndimcitira nsanje ndi ukali waukuru.
3 Atero Yehova: Ndabwerera kudza ku Ziyoni, ndidzakhala pakati pa Yerusalemu; ndi Yerusalemu adzachedwa, Madzi wa coonadi; ndi phiri la Yehova wa makamu, Phiri lopatulika.
4 Atero Yehova wa makamu: M'miseu ya Yerusalemu mudzakhalanso amuna ndi akazi okalamba, yense ndi ndodo yace m'dzanja lace cifukwa ca ukalamba wace.
5 Ndi m'miseu ya mudzi mudzakhala ana amuna ndi akazi akusewera m'miseu yace.
6 Atero Yehova wa makamu: Cikakhala codabwitsa pamaso pa otsala a anthu awa masiku awo, kodi cidzakhalanso codabwitsa pamaso panga? ati Yehova wa makamu.