28 ndipo zopanda pace za dziko lapansi, ndi zonyozeka, anazisankhula Mulungu, ndi zinthu zoti kulibe; 5 kuti akathere zinthu zoti ziriko;
29 6 kuti thupi liri lonse lisadzitamande pamaso pa Mulungu.
30 Koma kwa iye muli inu mwa Kristu Yesu, 7 amene anayesedwa kwa ife nzeru ya kwa Mulungu, ndi cilungamo ndi ciyeretso ndi ciombolo;
31 kuti monga mwalembedwa, iye amene adzitamanda, adzitamande mwa Ambuye.