3 Cisomo kwa inu ndi mtendere zocokera kwa Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Kristu.
4 Ndiyamika Mulungu wanga nthawi yonse kaamba ka inu, cifukwa ca cisomo ca Mulungu cinapatsidwa kwa inu mwa Kristu Yesu;
5 kuti m'zonse muoalemezedwa mwa iye, m'mau onse, ndi cidziwitso conse;
6 mongaumboni wa Kristu unakhazikika mwa inu;
7 kotero kuti sicikusowani inu caufuru ciri conse; pakulindira inu bvumbulutso la Ambuye wathu Yesu Kristu;
8 amenenso adzakukhazikitsani inu kufikira cimariziro, kuti mukhale opanda cifukwa m'tsiku la Ambuye: wathu Yesu Kristu.
9 Mulungu ali, wokhulupirika amene munaitanidwa mwa iye, ku ciyanjano ca Mwana wace Yesu Kristu, Ambuye wathu.