1 Pakuti sindifuna, kuti mukhale osadziwa, abale, kuti makolo athu onse anali pansi pa mtambo, naoloka nyanja onse;
2 nabatizidwa onse kwa Mose, mumtambo, ndi m'nyanja,
3 nadya onse cakudya cauzimu cimodzimodzi;
4 namwa onse cakumwa cauzimu cimodzimodzi; pakuti anamwa mwa thanthwe lauzimu lakuwatsata; koma thanthwelo ndiye Kristu.