11 Ngati ine tsono, kapena iwowa, kotero tilalikira, ndi kotero munakhulupira.
12 Koma ngati Kristu alalikidwa kuti waukitsidwa kwa akufa, nanga ena mwa inu anena bwanjikuti kulibe kuuka kwa akufa?
13 Koma ngati kulibe kuuka kwa akufa, Kristunso sanaukitsidwa;
14 ndipo ngati Kristu sanaukitsidwakulalikira kwathu kuli cabe, cikhulupiriro canunso ciri cabe.
15 Ndiponso ife tipezedwa mboni zonama za Mulungu; cifukwa n tinacita umboni kunena za Mulungu kuti anaukitsa Kristu; amene sanamuukitsa, ngati kuli tero kuti akufa saukitsidwa,
16 Pakuti ngati akufa saukitsidwa, Kristunso sanaukitsidwa;
17 ndipo ngati Kristu sanaukitsidwa, cikhulupiriro canu ciri copanda pace; muli cikhalire m'macimo anu.