3 Ndipo pamene ndifika, ndidzatuma iwo amene mudzawayesa oyenera, ndi akalata, apite nayo mphatso yanu ku Yerusalemu.
4 Ndipo ngati kuyenera kwa ine kupitanso, adzapita nane.
5 Koma ndidzadza kwa inu, nditapyola Makedoniya; pakuti ndidzapyola Makedoniya;
6 ndipo kapena ndidzakhalitsa ndi inu, kapenanso kugonera nyengo yacisanu kuti mukandiperekeze ine kumene kuli konse ndipitako,
7 Pakuti sindifuna kukuonani tsopano popitirira; pakuti ndiyembekeza kukhala ndi inu nthawi, ngati alola Ambuye.
8 Koma ndidzakhaia ku Efeso kufikira Penteskoste,
9 Pakuti panditsegukira pa khomo lalikuru ndi locititsa, ndipo oletsana nafe ndi ambiri.