1 Ndipo ine, abale, m'mene ndinadza kwa inu, sindinadza ndi kuposa kwa mau, kapena kwa nzeru, polalikira kwa inu cinsinsi ca Mulungu.
2 Pakuti ndinatsimikiza mtima kuti ndisadziwe kanthu mwa inu koma Yesu Kristu, ndi iye wopacikidwa.
3 Ndipo ine ndinakhala nanu mofoka ndi m'mantha, ndi monthunthumira mwambiri.
4 Ndipo mau anga ndi kulalikira kwanga sanakhala ndi mau okopa a nzeru, koma m'cionetso ca Mzimu ndi ca mphamvu;
5 kuti cikhulupiriro canu cisakhale m'nzeru ya anthu, koma mu mphamvu ya Mulungu.
6 Koma tilankhula nzeru mwa angwiro; koma si nzeru ya nthawi yino ya pansi pano, kapena ya akulu a nthawi yino ya pansi pano, amene alinkuthedwa;