4 Ndipo mau anga ndi kulalikira kwanga sanakhala ndi mau okopa a nzeru, koma m'cionetso ca Mzimu ndi ca mphamvu;
5 kuti cikhulupiriro canu cisakhale m'nzeru ya anthu, koma mu mphamvu ya Mulungu.
6 Koma tilankhula nzeru mwa angwiro; koma si nzeru ya nthawi yino ya pansi pano, kapena ya akulu a nthawi yino ya pansi pano, amene alinkuthedwa;
7 koma tilankhula nzeru ya Mulungu m'cinsinsi, yobisikayo, imene Mulungu anaikiratu, pasanakhale nyengo za pansi pano, ku ulemerero wathu,
8 imene saidziwa mmodzi wa akulu a nthawi a pansi pano; pakuti akadadziw sakadapaeika Mbuye wa ulemerero
9 koma monga kulembedwa,Zimene diso silinaziona, ndi khutu silinazimva,Nisizinalowa mu mtima wa munthu,Zimene ziri zonse Mulungi anakonzereratu iwo aku mkonda iye.
10 Koma kwa ife Mulungu anati onetsera izi mwa Mzimu; pakuti Mzimu asanthula zonse, zakuya za Mulungu zomwe.