17 Koma iye wophatikidwa ndi Ambuye ali mzimu umodzi.
18 Thawani dama. Cimo liri lonse munthu akalicita liri kunja kwa thupi; koma waciwerewere acimwira thupi lace la iye yekha.
19 Kapena simudziwa kuti thupi lanu liri kacisi wa Mzimu Woyera, amene ali mwa inu, amene muli naye kwa Mulungu? Ndipo simukhala a inu nokha.
20 Pakuti munagulidwa ndi mtengo wace wapatali; cifukwa cace lemekezani Mulungu m'thupi lanu.