1 Kodi sindine mfulu? Kodi slndine mtumwi? Kodi sindinaona Yesu Ambuye wathu? Kodi simuli inu nchito yanga mwa Ambuye?
2 Ngati sindiri mtumwi kwa ena, komatu ndiri kwa inu; pakuti cizindikilo ca utumwi wanga ndi inu mwa Ambuye.
3 Codzikanira canga kwa iwoamene andifunsa ine ndi ici:
4 Kodi tiribe ulamuliro wa kudya ndi kumwa?