7 kotero kwina kuti inu mumkhululukire ndi kumtonthoza, kuti wotereyo mgamizidwe ndi cisoni cocurukaco.
8 Cifukwa cace ndikupemphani inu kuti mumtsimikizire ameneyo cikondi canu.
9 Pakuti cifukwa ca ici ndalembanso, kuti ndidziwe mayesedwe anu, ngati muli omvera m'zonse.
10 Koma amene mumkhululukira kanthu, inenso nditero naye; pakuti cimene ndakhululukira inenso, ngati ndakhululukira kanthu, ndacicita cifukwa ca inu, pamasopa Kristu;
11 kuti asaticenierere Satana; pakuti sitikhala osadziwa macenjerero ace.
12 Koma pamene ndinadza ku Trowa kudzalalikira Uthenga Wabwino wa Kristu, ndipo pamene padanditsegukira kwa ine pakhomo, mwa Ambuye,
13 ndinalibe mpumulo mu mzimu wanga, posapeza ine Tito mbale wanga; koma polawirana nao ndinanka ku Makedoniya.