2 Akorinto 1 BL92

1 PAULO, mtumwi wa Kristu Yesu, mwa cifuniro ca Mulungu, ndi Timoteo mbaleyo, kwa Mpingo wa Mulungu umene uli ku Korinto, pamodzi ndi oyera mtima onse amene ali m'Akaya lonse:

2 Cisomo kwa inu ndi mtendere zocokera kwa Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Kristu.

Ciyamiko pa matonthozo a Mulungu

3 Wolemekezeka Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Kristu, Atate wa zifundo ndi Mulungu wa citonthozo conse,

4 woo titonthoza ife m'nsautso yathu yonse, kuti tidzathe ife kutonthoza iwo okhala m'nsautso iri yonse, mwa citonthozo cimene titonthozedwa naco tokha ndi Mulungu.

5 Pakuti monga masautso a Kristu aticurukira ife, coteronso citonthozo cathu cicuruka mwa Kristu,

6 Koma ngati tisautsidwa, kuli cifukwa ca citonthozo ndi cipulumutso canu; ngati titonthozedwa, kuli kwa citonthozo canu cimene cicititsa mwa kupirira kwa masautso omwewo amene ifenso timva.

7 Ndipo ciyembekezo cathu ca kwa inu ncokbazikika; podziwa kuti monga muli oyanjana ndi masautsowo, koteronso ndi citonthozo.

8 Pakuti sitifuna abale, kuti mukhale osadziwa za cisautso cathu tinakomana naco m'Asiya, kuti tinathodwa kwakukuru, koposa mphamvu yathu, kotero kuti tinada nkhawa ngakhale za moyo wathu;

9 koma tokha tinakhala naco citsutso ca imfa mwa ife tokha, kuti tisalimbike pa ife tokha, koma pa Mulungu wakuukitsa akufa;

10 amene anatilanditsa mu imfa yaikuru yotere, nadzalanditsa;

11 amene timyembekezera kuti adzalanditsanso; pothandizana inunso ndi pemphero lanu la kwa ife; kuti pa mphatso ya kwa ife yodzera kwa anthu ambiri, payamikike ndi anthu ambiri cifukwa ca ife.

Cifukwa ca kucedwa Paulo kudza ku Korinto

12 Pakuti kudzitamandira kwathu ndiko umboni wa cikumbu mtima cathu, kuti m'ciyero ndi kuona mtima kwa Mulungu, si m'nzeru ya thupi, koma m'cisomo ca Mulungu tinadzisunga m'dziko lapansi, koma koposa kwa inu.

13 Pakuti sitilemba kwa inu zina, koma zimene muwerenga, kapenanso mubvomereza; ndipo ndiyembekeza kuti mudzabvomereza kufikira cimariziro;

14 monganso munatibvomerezera ife pena, kuti ife ndife kudzitamandira kwanu, monga momwe inunso muli kudzitamandira kwathu m'tsiku la Ambuye wathu Yesu.

15 Ndipo m'kulimbika kumene ndinafuna kudza kwa inu kale, kuti mukakhalenaco cisomo caciwiri;

16 ndipo popyola kwanu kupita ku Makedoniya, ndi kudzanso kwa inu pobwera kufuma ku Makedoniya; ndi kuperekezedwa ndi inu ku Yudeya.

17 Pamenepo, pakufuna cimene, kodi ndinacitapo kosinthasintha? Kapena zimene nditsimikiza mtima kodi ndizitsimikiza mtima monga mwa thupi? Kuti pa ine pakhale eya, eya, ndi iai, iai?

18 Koma Mulungu ali wokhulupirika, kuti mau athu a kwa inu sanakhala eya ndi iai.

19 Pakuti Mwana wa Mulungu, Yesu Kristu, amene analalikidwa mwa inu ndi ife, (ine ndi Silvano ndi Timoteo) sanakhala eya ndi iai, koma anakhala eya mwa iye.

20 Pakuti monga mawerengedwe a malonjezano a Mulungu ali mwa iye eya; cifukwa cacenso ali mwa iye Amen, kwa ulemerero wa Mulungu mwa ife.

21 Koma iye wakutikhazika pamodzi ndi inu kwa Kristu, natidzoza ife, ndiye Mulungu;

22 amenenso anatisindikiza cizindikilo, natipatsa cikole ca Mzimu mu mitima yathu.

23 Koma ine ndiitana Mulungu akhale mboni pa moyo wanga, kud kulekera inu ndinaleka kudza ku Korinto.

24 Si kuti ticita ufumu pa cikhulupiriro canu, koma tikhala othandizana naco cimwemwe canu; pakuti ndi cikhulupiriro muimadi.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13