2 Akorinto 11 BL92

Za atumwi onyenga

1 Mwenzi mutandilola pang'ono ndi copusaco! Komanso mundilole.

2 Pakuti ndicita nsanje pa inu ndi nsanje ya Mulungu; pakuti ndinakupalitsani ubwenzi mwamuna mmodzi, kuti ndikalangize inu ngati namwali woyera mtima kwa Kristu.

3 Koma ndiopa, kuti pena, monga njoka inanyenga Heva ndi kucenjerera kwace, maganizo anu angaipsidwe kusiyana nako kuona mtima ndi kuyera mtima ziri kwa Kristu.

4 Pakutitu ngati iye wakudza alalikira Yesu wina, amene ife sitinalalikira, kapena ngati mulandira mzimu wa mtundu wina, umene simunalandira, kapena uthenga wabwino wa mtundu wina umene simunalandira, mulolana nave bwino lomwe.

5 Pakuti ndiyesa kuti sindinaperewera konse ndi atumwi oposatu,

6 Ndipo ndingakhale ndiri wosaphunzira m'manenedwe, koma sinditero m'cidziwitso, koma m'zonse tacionetsa kwa inu mwa anthu onse.

7 Kodi ndacimwa podzicepetsa ndekha, kuti inu mukakwezedwe, popeza ndinalalikira kwa inu Uthenga Wabwino wa Mulungu mwaufulu?

8 ndinalanda za Mipingo yina, ndi kulandira kwa iwo kulipira kuti ndikatumikire inu;

9 ndipo pakukhala nanu, ndi kusowa, sindinasaukitsa munthu ali yense; pakuti abale akucokera ku Makedoniya, anakwaniritsa kusowa kwanga; ndipo m'zonse ndinacenjera ndekha, ndisalemetse inu, ndipo ndidzacenjerapo.

10 Coonadi ca Kristu ciri mwa ine, kuti kudzitamandira kumene sikudzaletsedwa kwa ine mu mbali za Akaya,

11 Cifukwa ninji? Cifukwa sindikonda inu kodi? Adziwa Mulungu.

12 Koma cimene ndicita, ndidzacitanso, kuti ndikawadulire cifukwa iwo akufuna cifukwa; kuti m'mene adzitamandiramo, apezedwe monganso ife.

13 Pakuti otere ali atumwi onyenga, ocita ocenjerera, odzionetsa ngati atumwi a Kristu,

14 Ndipo kulibe kudabwa; pakuti Satana yemwe adzionetsa ngati mngelo wa kuunika.

15 Cifukwa cace sikuli kanthu kwakukuru ngatinso atumiki ace adzionetsa monga atumiki a cilungamo; amene cimariziro cao cidzakhala monga nchito zao.

Kumva zowawa kwa Paulo cifukwa ca Uthenga Wabwino

16 Ndinenanso, Munthu asandiyese wopanda nzeru; koma ngati mutero, mundilandirenso ine monga wopanda nzeru, kuti inenso ndidzitamandire pang'ono.

17 Cimene ndilankhula sindilankhula monga mwa Ambuye, koma monga wopanda nzeru, m'kulimbika kumene kwa kudzitamandira.

18 Popeza ambiri adzitamandira monga mwa thupi, inenso ndidzadzitamandira.

19 Pakuti mulolana nao opanda nzeru mokondwera, pokhala anzeru inu nokha.

20 Pakuti mulola ngati wina akuyesani inu akapolo, ngati wina alikwira inu, ngati wina alanda zanu, ngati wina adzikuza, ngati wina akupandani pankhope.

21 Ndinena monga mwa kunyoza, monga ngati tinakhala ofoka. Koma m'mene wina alimbika mtimamo (ndinena mopanda nzeru) momwemo ndilimbika mtima inenso.

22 Kodi ali Ahebri? Inenso. Kodi ali Aisrayeli? Inenso. Kodi ali mbeu ya Abrahamu? Inenso.

23 Kodi ali atumiki a Kristu? (ndilankhula monga moyaruka), makamaka ine; m'zibvutitso mocurukira, m'ndende mocurukira, m'mikwingwirima mosawerengeka, muimfa kawiri kawiri.

24 Kwa Ayuda ndinalandirakasanu mikwingwirima makumi anai kuperewera umodzi.

25 Katatu ndinamenyedwa ndi ndodo, kamodzi ndinaponyedwa miyala, katatu ndinatayika posweka combo, ndinakhala m'kuya tsiku limodzi usana ndi usiku;

26 paulendo kawiri kawiri, moopsya mwace mwa mitsinje, moopsya mwace mwa olanda, 1 moopsya modzera kwa mtundu wanga, moopsya modzera kwa amitundu, moopsya m'mudzi, moopsya m'cipululu, moopsya m'nyanja, moopsya mwaabale onyenga;

27 m'cibvutitso ndi m'colemetsa, m'madikiro kawiri kawiri, 2 m'njala ndi ludzu, m'masalo a cakudyakawiri kawiri, m'cisanu ndi umarisece.

28 Popanda zakunjazo pali condisindikiza tsiku ndi tsiku, calabadiro ca Mipingo yonse.

29 3 Afoka ndani wosafoka inenso? Akhumudwitsidwa ndani, wosatenthanso ine?

30 Ngati ndiyenerakudzitamandira, 4 ndidzadzitamandira ndi za kufoka kwanga.

31 Mulungu Atate wa Ambuye Yesu, iye amene alemekezeka ku nthawi yonse, adziwa kuti sindinama.

32 M'Damasiko kazembe wa mfumu Areta analindizitsa mudzi wa Adamasiko kuti andigwire ine;

33 ndipo mwa zenera, mumtanga, ananditsitsa pakhoma, ndipo ndinapulumuka m'manja mwace.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13