5 kuti cikhulupiriro canu cisakhale m'nzeru ya anthu, koma mu mphamvu ya Mulungu.
6 Koma tilankhula nzeru mwa angwiro; koma si nzeru ya nthawi yino ya pansi pano, kapena ya akulu a nthawi yino ya pansi pano, amene alinkuthedwa;
7 koma tilankhula nzeru ya Mulungu m'cinsinsi, yobisikayo, imene Mulungu anaikiratu, pasanakhale nyengo za pansi pano, ku ulemerero wathu,
8 imene saidziwa mmodzi wa akulu a nthawi a pansi pano; pakuti akadadziw sakadapaeika Mbuye wa ulemerero
9 koma monga kulembedwa,Zimene diso silinaziona, ndi khutu silinazimva,Nisizinalowa mu mtima wa munthu,Zimene ziri zonse Mulungi anakonzereratu iwo aku mkonda iye.
10 Koma kwa ife Mulungu anati onetsera izi mwa Mzimu; pakuti Mzimu asanthula zonse, zakuya za Mulungu zomwe.
11 Pakuti ndani wa anthu adziwa za munthu, koma mzimu wa munthuyu uli mwa iye? momwemonso za Mulungu palibe wina azidziwa, koma Mzimu wa Mulungu.