18 Kodi waitanidwa wina wodulidwa? Asakhale wosadulidwa. Kodi waitanidwa wina wosadulidwa? Asadulidwe.
19 Mdulidwe ulibe kanthu, ndi kusadulidwa kulibe kanthu, koma kusunga kwa malamulo a Mulungu.
20 Yense akhale m'maitanidwe m'mene anaitanidwamo.
21 Kodi unaitanidwa uli kapolo? Usasamalako; koma ngati ukhozanso kukhala mfulu, cita nako ndiko.
22 Pakuti iye amene anaitanidwa mwa Ambuye, pokhala ali kapolo, ali mfulu ya Ambuye: momwemonso woitanidwayo, pokhala ali mfulu, ali kapolo wa Kristu.
23 Munagulidwa ndi mtengo wace; musakhale akapolo a anthu.
24 Yense, m'mene anaitanidwamo, abate, akhale momwemo ndi Mulungu.