4 Kodi tiribe ulamuliro wa kudya ndi kumwa?
5 Kodi tiribe ulamuliro wakuyendayenda naye mkazi, ndiye mbale, monganso atumwi ena, ndi abale a Ambuye, ndi Kefa?
6 Kapena kodi ife tokha, Bamaba ndi ine, tiribe ulamuliro wakusagwira nchito?
7 Msilikari ndani acita nkhondo, nthawi iriyonse, nadzifunira zace yekha? Aoka mipesa ndani, osadya cipatso cace? Kapena aweta gulu ndani, osadyamkaka wace wa gululo? Kodi ndilankhula izi monga mwa anthu?
8 Kapena cilamulo sieinenanso zomwezo?
9 Pakuti m'cilamulo ca Mose mwalembedwa, Usapunamitsa ng'ombe pakupuntha iyo dzinthu. Kodi Mulungu asamalira ng'ombe?
10 Kapena acinena ici konse konse cifukwa ca ife? Pakuti, cifukwa ca ife kwalembedwa: popeza wolima ayenera kulima mwa ciyembekezo, ndi wopunthayo acita mwa ciyembekezo ca kugawana nao.