3 Mwamunayo apereke kwa mkazi mangawa ace; koma modzimodzinso mkazi kwa mwamuna.
4 Mkazi alibe ulamuliro wa pa thupi lace la iye yekha, koma mwamuna ndiye; koma momwemonso mwamuna alibe ulamuliro wa pa thupi laiye yekha, koma mkazi ndiye.
5 Musakanizana, koma ndi kubvomerezana kwanu ndiko, kwa nthawi, kuti mukadzipereke kwa kupemphera, nimukakhalenso pamodzi, kuti Satana angakuyeseni, cifukwa ca kusadziletsa kwanu.
6 Koma ici ndinena monga mwa kulola, si monga mwa kulamulira.
7 Koma mwenzi anthu onse akadakhala monga momwe ndiri ine ndekha. Koma munthu yense ali nayo mphatso yace ya iye yekha kwa Mulungu, wina cakuti, wina cakuti.
8 Koma ndinena kwa osakwatira, ndi kwa akazi amasiye, kuti kuli bwino kwa iwo ngati akhala monganso ine.
9 Koma ngati sadziwa kudziletsa, akwatitsidwe; pakuti nkwabwino kukwatira koposa kutentha mtima.