1 Koma za zoperekedwa nsembe kwa mafano: Tidziwa kuti tid naco cidziwitso tonse. Cidziwitso citukumula, koma cikondicimangirira.
2 Ngati wina ayesa kuti adziwa kanthu sanayambe kudziwa monga ayenera kudziwa.
3 Koma ngati wina akonda Mulungu, yemweyu adziwika ndi iye.
4 Tsono kunena za kudya zoperekedwa nsembe kwa mafano, tidziwa kuti fano siliri kanthu pa dziko lapansi, ndi kuti palibe Mulungu koma mmodzi.