12 Cotero imfa icita mwa ife, koma moyo mwa inu.
13 Koma pokhala nao mzimu womwewo wa cikhulupiriro, monga mwa colembedwaco, ndinakhulupira, cifukwa cace ndinalankhula; ifenso tikhulupira, cifukwa cace tilankhula;
14 podziwa kuti iye amene anaukitsa Ambuye Yesu adzaukitsa ifenso pamodzi ndi Yesu, nadzatiikapo pamodzi ndi inu.
15 Pakuti zonsezi nza kwa inu, kuti cisomoco, cocurukitsidwa mwa unyinjiwo, cicurukitsire ciyamiko ku ulemerero wa Mulungu.
16 Cifukwa cace sitifoka; koma ungakhale umunthu wathu wakunja ubvunda, wa m'kati mwathu ukonzedwa kwatsopano tsiku ndi tsiku.
17 Pakuti cisautso cathu copepuka ca kanthawi citicitira ife kulemera koposa kwakukuru ndi kosatha kwa ulemerero;
18 popeza sitipenyerera zinthu zooneka, koma zinthu zosaoneka; pakuti zinthu zooneka ziri za nthawi, koma zinthu zosaoneka ziri zosatha.