2 umene iye analonjeza kale ndi mau a ananeri ace m'malembo oyera,
3 wakunena za Mwana wace, amene anabadwa, wa mbeu ya Davide, monga mwa thupi,
4 amene anatsimikizidwa ndi mphamvu kuti ndiye Mwana wa Mulungu monga mwa Mzimu wa ciyero, ndi kuuka kwa akufa; ndiye Yesu Kristu Ambuye wathu;
5 amene ife tinalandira naye cisomo ndi utumwi, kuti amvere cikhulupiriro anthu a mitundu yonse cifukwa ca dzina lace;
6 mwa amenewo muli inunso, oitanidwa a Yesu Kristu;
7 kwa onse a ku Roma, okondedwa a Mulungu, oitanidwa kuti akhale oyera mtima: Cisomo cikhale ndinu ndi mtendere wa kwa Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Kristu.
8 Poyamba, ndiyamika Mulungu wanga mwa Yesu Kristu cifukwa ca inu nonse, cifukwa kuti mbiri ya cikhulupiriro canu idamveka pa dziko lonse lapansi.