Aroma 13 BL92

Kugonjera kwathu kwa akuru

1 Anthu onse amvere maulamuliro a akulu; pakuti palibe ulamuliro wina koma wocokera kwa Mulungu; ndipo iwo amene alipo aikidwa ndi Mulungu.

2 Kotero kuti iye amene atsutsana nao ulamuliro, akaniza coikika ndi Mulungu; ndipo iwo akukaniza, adzadzitengera kulanga

3 Pakuti mafumu sakhala oopss nchito zabwino koma zoipa. Ndipo ufuna kodi kusaopa ulamuliro: Cita cabwino, ndipo udzalandirs kutama m'menemo:

4 pakuti ndiye mtumiki wa Mulungu, kucitira iwe zabwino. Koma ngati ucita coipa opatu, pakuti iye sagwira lupanga kwacabe; pakuti ndiye mtumiki wa Mulungu wakukwiyira ndi kubwe zera cilango wocita zoipa.

5 Cifukwa cace, kuyenera kuti mukhale omvera, si cifukwa ca mkwiyo woo kha, komanso cifukwa ca cikumbu mtima.

6 Pakuti cifukwa ca ici mupatsanso msonkho; pakuti iwo ndi wo atumiki a Mulungu akulabadira be cinthu cimeneci.

7 Perekani kwa anthu onse mangawa ao; msonkho kwa eni ace a msonkho; kuli pira kwa eni ace a kulipidwa; kuopa kwa eni ace a kuwaopa; ulemu kwe eni ace a ulemu.

Kukondana, kudikira, ciyero

8 Musakhale ndi mangawa kwa munthu ali yense, koma kukondana ndiko; pakuti iye amene akondana ndi mnzace wakwanitsa lamulo.

9 Pakuti ili, Usacite cigololo, Usaphe, Usabe, Usasirire, ndipo lingakhale lamulo lina liri lonse, limangika pamodzi m'mau amenewa, kuti, Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe wekha.

10 Cikondano sicicitira mnzace coipa; cotero cikondanoco ciri cokwanitsa lao mulo.

11 Ndipo citani ici, podziwa inu nyengo, kuti tsopano ndiyo nthawi yabwino yakuuka kutulo; pakuti tsopano cipulumutso cathu ciri pafupi koposa pamene tinayamba kukhulupira.

12 Usiku wapita, ndi dzuwa layandikira; cifukwa cace tibvule nchito za mdima, ntibvale camuna ca kuunika.

13 Tiyendeyeode koyenera, monga usana; si m'madyerero ndi kuledzera ai, si m'cigololo ndi conyansa ai, si mu ndeu ndi nkhwidzi ai.

14 Koma bvalani inu Ambuye Yesu-Kristu, ndipo musaganizire za thupi kucita zofuna zace.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16