10 Maso ao adetsedwe, kuti asapenye,Ndipo muweramitse msana wao masiku onse.
11 Cifukwa cace ndinena, Anakhumudwa kodi kuti agwe? Msatero ai; koma ndi kulakwa kwao cipulumutso cinadza kwa anthu akunja, kudzacititsa iwo nsanje.
12 Ndipo ngati kulakwa kwao kwatengera dzikolapansi zolemera, ndipo kucepa kwao klltengera anthu amitundu zolemera; koposa kotani nanga kudzaza kwao?
13 Koma ndilankhula ndi inu anthu amitundu. Popeza ine ndiri mtumwi wa anthu amitundu, millemekeza utumiki wanga;
14 kuti ngati nkutheka ndikacititse nsanje amenewo a mtundu wanga; ndi kupulumutsa ena a iwo.
15 Pakuti ngati kuwataya kwao kuli kuvanianitsa kwa dziko lapansi, nanga kulandiridwa kwao kudzatani, koma ndithu ngati moyo wakucokera kwa: akufa?
16 Ndipo ngati zoundukula ziri zopatulika, coteronso mtanda; ndipo ngati muzu uli wopatulika, coteronso nthambi.