17 Musabwezere munthu ali yense coipa cosinthana ndi coipa. Ganiziranitu zinthu za ulemu pamaso pa anthu onse.
18 Ngati nkutheka, monga momwe mukhoza, khalani ndi mtendere ndi anthu onse.
19 Musabwezere coipa, okondedwa, koma patukani pamkwiyo; pakuti kwalembedwa, Kubwezera kuli kwanga, Ine ndidzabwezera, ati Ambuye.
20 Koma ngati mdani wako akumva njala, umdyetse, ngati akumva ludzu, ummwetse; pakuti pakutero udzaunjika makala a mota pamutu pace.
21 Musagonje kwa coipa, koma ndi cabwino genietsani coipa.