4 Pakuti monga m'thupi limodzi tiri nazo ziwalo zambiri, ndipo ziwalo zonsezo siziri nayo nchito imodzimodzi;
5 comweco ife, ndife ambiri, tiri thupi limodzi mwa Kristu, ndi ziwalo zinzace, wina ndi wina.
6 Ndipo pokhala ife ndi mphatso zosiyana, monga mwa cisomo copatsidwa kwa ife, kapena mphatso yakunenera, tinenere monga mwa muyeso wa cikhulupiriro;
7 kapenayakutumikira, tidzipereke ku utumiki uwu; kapena iye wakuphunzitsa, kukuphunzitsako;
8 kapena iye wakudandaulira, kukudandaulirako; wakugawira acite ndi mtima woona; iye wakuweruza, aweruze ndi cangu; iye wakucita cifundo, acite ndi kukondwa mtima.
9 Cikondano cikhale copanda cinyengo, Dana naco coipa; gwirizana naco cabwino.
10 M'cikondano ca anzanu wina ndi mnzace mukondane ndi cikondi ceni ceni; mutsogolerane ndi kucitira wina mnzace ulemu;