6 Iye wakusamalira tsiku, alisamalira kwa Ambuye: ndipo iye wakudya, adya mwa Ambuye, pakuti ayamika Mulungu; ndipo iye wosadya, mwa Ambuye sakudya, nayamikanso Mulungu.
7 Pakuti palibe mmodzi wa ife adzikhalira ndi moyo yekha, ndipo palibe mmodzi adzifera yekha.
8 Pakuti tingakhale tiri ndi moyo, tikhalira Ambuye moyo; kapena tikafa, tifera Ambuye; cifukwa cace tingakhale tiri ndi moyo, kapena tikafa, tikhala ace a Ambuye.
9 Pakuti, cifukwa ca ici Kristu adafera, nakhalanso ndi moyo, kuti iye akakhale Ambuye wa akufa ndi wa amoyo.
10 Koma iwe uweruziranji mbale wako? kapena iwenso upeputsiranji mbale wako? pakuti ife tonse tidzaimirira ku mpando wakuweruza wa Mulungu.
11 Pakuti kwalembedwa,Pali moyo wanga, ari Ambuye, mabondo onse adzagwadira Ine,Ndipo malilime onse adzabvomereza Mulungu,
12 Cotero munthu ali yense wa ife adzadziwerengera mlandu wace kwa Mulungu.