17 Ndipo ndikudandaulirani; abale, yang'anirani iwo akucita zopatutsana ndi zopunthwitsa, kosalingana ndi ciphunzitsoco munaciphunzira inu; ndipopotolokani pa iwo.
18 Pakuti otere satumikira Ambuye wathu Kristu, koma mimba yao; ndipo ndi mau osalaza ndi osyasyalika asoceretsamitiina ya osalakwa.
19 Pakuti kumvera kwanu kunabuka kwa anthu onse. Cifukwa cace ndikondwera ndi inu; koma ndifuna kuti mukakhale anzeru pa zabwino, koma ozungulidwa pa zoipa.
20 Ndipo Mulungu wa mtendere adzaphwanva: Satana pansi pa mapazi anu tsopano lino.Cisomo ca Ambuye wathu Yesu Kristu cikhale ndi inu nonse.
21 Timoteo wanchito mnzanga akulankhulani inu; ndi Lukiyo ndi Yasoni ndi Sosipatro, abale anga.
22 Ine Tertio, ndirikulemba kalata ameneyu, ndikulankhulani inu mwa Ambuye.
23 Gayo, mwini nyumba wolandira ine, ndi Eklesia yense wa Ambuye, akulankhulani inu. Erasto, ndiye woyang'anira mudzi, akulankhulani inu, ndiponso Kwarto mbaleyo.