4 amene anapereka khosi lao cifukwa ca moyo wanga; amene ndiwayamika, si ine ndekha, komanso Mipingo yonse ya Ambuye ya kwa anthu amitundu;
5 ndipo mulankhule Mpingo wa Ambuye wa m'nyumba mwao. Mulankhule Epeneto wokondedwa wanga, ndiye cipatso coundukula ca Asiya ca kwa Kristu,
6 Mulankhule Mariya amene anadzilemetsa ndi nchito zambiri zothandiza inu.
7 Mulankhule Androniko ndi Yuniya, anansi anga, ndi andende anzanga, amene ali omveka mwa amitumwi, amenenso ananditsogolera ine mwa Kristu.
8 Mulankhule Ampliato wokondedwa wanga mwa Ambuye.
9 Mulankhule Urbano wanchito mnzathu mwa Kristu, ndi Staku wokondedwa wanga,
10 Mulankhule Apele, wobvomerezedwayo mwa Kristu, Mulankhule iwo a kwa Aristobulo.