6 Mulankhule Mariya amene anadzilemetsa ndi nchito zambiri zothandiza inu.
7 Mulankhule Androniko ndi Yuniya, anansi anga, ndi andende anzanga, amene ali omveka mwa amitumwi, amenenso ananditsogolera ine mwa Kristu.
8 Mulankhule Ampliato wokondedwa wanga mwa Ambuye.
9 Mulankhule Urbano wanchito mnzathu mwa Kristu, ndi Staku wokondedwa wanga,
10 Mulankhule Apele, wobvomerezedwayo mwa Kristu, Mulankhule iwo a kwa Aristobulo.
11 Mulankhule Herodiona, mbale wanga. Mulankhule iwo a kwa Narkiso, amene ali mwa Ambuye.
12 Mulankhule Trufena, ndi Trufosa amene agwiritsa nchito mwa Ambuyeo Mulankhule. Persida, wokondedwayo amene anagwiritsa nchito zambiri mwa Ambuye.