10 monga kwalembedwa,Palibe mmodzi wolungama, inde palibe mmodzi;
11 Palibe mmodzi wakudziwitsa, Palibe mmodzi wakuloodola Mulungu;
12 Onsewa apatuka, pamodzi akhala opanda pace;Palibe mmodzi wakucita zabwino, inde, palibe mmodzi ndithu.
13 M'mero mwao muli manda apululu;Ndi lilime lao amanyenga; Ululu wa mamba uli pansi pa milomo yao;
14 M'kamwa mwao mudzala ndi zotemberera ndi zowawa;
15 Miyendo yao icita liwiro kukhetsa mwazi;
16 Kusakaza ndi kusauka kuli m'njira zao;