34 Ndipo anaciritsa anthu ambiri akudwala nthenda za mitundu mitundu, naturutsa ziwanda zambiri; ndipo sanalola ziwandazo zilankhule, cifukwa zinamdziwa Iye.
35 Ndipo m'mawa mwace anauka usikusiku, naturuka namuka kucipululu, napemphera kumeneko.
36 Ndipo Simoni ndi anzace anali naye anamtsata,
37 nampeza, nanena naye, Akufunani inu anthu onse.
38 Ndipo ananena nao, Tiyeni kwina, ku midzi iri pafupi apa, kuti ndilalikire komwekonso; pakuti ndadzera nchito imene.
39 Ndipo analowa m'masunagoge mwao m'Galileya monse, nalalikira, naturutsa ziwanda.
40 Ndipo anadza kwa Iye wodwala khate, nampempha Iye, namgwadira, ndi kunena ndi Iye, Ngati mufuna mukhoza kundikonza.