Marko 2 BL92

Aciritsa wodwala manjenje

1 Ndipo polowanso Iye m'Kapernao atapita masiku ena, kunamveka kuti ali m'nyumba.

2 Ndipo ambiri anaunjikana, kotero kuti anasowa malo, ngakhale pakhomo pomwe; ndipo analankhula nao mau.

3 Ndipo anadza kwa Iye otenga munthu wodwala manjenje, wonyamulidwa ndi anthu anai.

4 Ndipo pamene sanakhoza kufika kuli Iye, cifukwa ca khamu la anthu, anasasula chindwi pokhala Iye; ndipo pamene anatha kuliboola, anatsitsa mphasa m'mene alinkugonamo wodwala manjenjeyo,

5 Ndipo Yesu pakuona cikhulupiriro cao ananena ndi wodwala manjenje, Mwana, macimo ako akhululukidwa.

6 Koma anakhalapo ena a alembi akuganizira mumtima mwao,

7 Munthu amene atero bwanji? acita mwano; akhoza ndani kukhululukira macimo, koma mmodzi, ndiye Mulungu?

8 Ndipo pomwepo Yesu pozindikira mumtima mwace kuti alikuganizira comweco mwa iwo okha, ananena nao, Muganiza bwanji zinthu izi m'mitima yanu?

9 Capafupi nciti, kapena kuuza wodwala manjenje kuti, Macimo ako akhululukidwa; kapena kuti, Nyamuka, senza mphasa yako, nuyende?

10 Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa munthu ali mwini ulamuliro wakukhululukira macimo pa dziko lapansi (ananena ndi wodwala manjenje),

11 Ndikuuza iwe, Nyamuka, senza mphasa yako, numuke kwanu.

12 Ndipo ananyamuka iye pomwepo, nasenza mphasa, naturuka pamaso pa iwo onse; kotero kuti anadabwa onse, nalemekeza Mulungu, nanena kuti, Zotere sitinaziona ndi kale lonse.

Yesu aitana Levi

13 Ndipo anaturukanso kunka m'mbali mwa nyanja; ndipo linadza kwa Iye khamu lonse la anthu, ndipo anawaphunzitsa.

14 Ndipo pakumuka, anaona Levi mwana wa Alifeyu alikukhala polandira msonkho, ndipo ananena naye, Tsata Ine.

15 Ndipo ananyamuka namtsata Iye. Ndipo kunali kuti anakhala pakudya m'nyumba mwace, ndipo amisonkho ndi ocimwa ambiri anakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ace, pakuti anali ambiri, ndipo anamtsata Iye.

16 Ndipo alembi a kwa Afarisi, pakuona kuti alinkudya nao ocimwa ndi amisonkho, ananena ndi ophunzira ace, Uyu akudya ndi kumwa nao amisonkho ndi ocimwa.

17 Ndipo pamene Yesu anamva ici, ananena nao, Akulimba safuna sing'anga, koma odwala ndiwo; sindinadza kudzaitana olungama, koma ocimwa.

Kudzikana kudya

18 Ndipo ophunzira a Yohane ndi Afarisi analinkusala kudya; ndipo anadza, nanena ndi Iye, Bwanji asala kudya ophunzira a Yohane, ndi ophunzira a Afarisi, koma ophunzira anu sasala kudya?

19 Ndipo Yesu ananena nao, Kodi akhoza kusala kudya anyamata a ukwati pamene mkwati ali pamodzi nao? pokhala ali naye mkwati pamodzi ndi iwo sakhoza kusala.

20 Koma adzadza masiku, pamene mkwati adzacotsedwa kwa iwo, ndipo pamenepo adzasala kudya tsiku lomwelo.

21 Palibe munthu asokerera cigamba ca nsaru yaiwisi pa copfunda cakale; pena cimene coti cidzakonza cizomolapo, catsopanoco cizomoka pa cakaleco, ndipo ciboo cikulapo.

22 Ndipo palibe munthu amatsanulira vinyo watsopano m'matumba akale: pena vinyo adzaphulitsa matumba, ndipo aonongeka vinyo, ndi matumba omwe: koma vinyo watsopano amatsanulira m'matumba atsopano.

Yesu mwini Sabata

23 Ndipo kunali kuti anapita Iye pakati pa minda dzuwa la Sabata; ndipo ophunzira ace poyenda anayamba kubudula ngala za dzinthu.

24 Ndipo Afarisi ananena ndi Iye, Taona, acitiranji cosaloleka kucitika dzuwa la Sabata?

25 Ndipo ananena nao, Simunawerenga konse cimene anacicita Davide, pamene adasowa, namva njala, iye ndi iwo amene anali pamodzi naye?

26 Kuti, analowa m'nyumba ya Mulungu masiku a Abyatara, mkulu wa ansembe, ndipo anadya mikate yoonetsera, yosaloleka kudya ena, koma ansembe okha, ndipo anawapatsanso iwo amene anali naye?

27 Ndipo ananena nao, Sabata linaikidwa cifukwa ca munthu, si munthu cifukwa ca Sabata;

28 motero Mwana wa munthu ali mwini dzuwa la Sabata lomwe.

Mitu

1 2 3 4 5 6 7 8 9 10 11 12 13 14 15 16