40 Ndipo anadza kwa Iye wodwala khate, nampempha Iye, namgwadira, ndi kunena ndi Iye, Ngati mufuna mukhoza kundikonza.
41 Ndipo Yesu anagwidwa cifundo, natansa dzanja namkhudza iye, nanena naye, Ndifuna; khala wokonzedwa.
42 Ndipo pomwepo khate linamcoka, ndipo anakonzedwa.
43 Ndipo anamuuzitsa, namturutsa pomwepo,
44 nanena naye, Ona, usati unene kanthu kwa munthu ali yense: koma muka, ukadzionetse kwa wansembe, nupereke pa makonzedwe ako 1 zimene adalamulira Mose, zikhale mboni kwa iwo.
45 Koma 2 iye anaturuka nayamba kulalikira ndithu, ndi kubukitsa mauwo, kotero kuti Yesu sanadziwa kulowansopoyera m'mudzi, koma anakhala padera m'mapululu; ndipo anadza kwa Iye anthu a ku malo onse.