30 amene sadzalandira makumi khumi tsopano nthawi yino, nyumba, ndi abale, ndi alongo, ndi amai, ndi ana, ndi minda, pamodzi ndi mazunzo; ndipo nthawi irinkudza, moyo wosatha.
31 Koma ambiri akuyamba adzakhala akuthungo, ndi akuthungo adzakhala oyamba.
32 Ndipo iwo anali m'njira alinkukwera kunka ku Yerusalemu; ndipo Yesu analikuwatsogolera; ndipo iwo anazizwa; ndipo akumtsatawo anacita mantha. Ndipo Iye anatenganso khumi ndi awiriwo, nayamba kuwauza zinthu zimene zidzamfikira Iye,
33 nati, Taonani, tikwera ku Yerusalemu; ndipo Mwana wa munthu adzaperekedwa kwa ansembe akuru ndi alembi; ndipo iwo adzamweruza kuti ayenera imfa, nadzampereka Iye kwa anthu a mitundu;
34 ndipo adzamnyoza Iye, nadzamthira malobvu, nadzamkwapula Iye, nadzamupha; ndipo pofika masiku atatu adzauka.
35 Ndipo anadza kwa Iye Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, nanena naye, Mphunzitsi, tifuna kuti mudzaticitire cimene ciri conse tidzapempha kwa Inu.
36 Ndipo Iye anati kwa iwo, Mufuna kuti ndidzakucitireni inu ciani?