4 Ndipo anati, Mose analola kulembera kalata wakulekanira, ndi kumcotsa.
5 Koma Yesu anati kwa iwo, Cifukwa ca kuuma kwa mitima yanu anakulemberani lamulo ili.
6 Koma kuyambira pa ciyambi ca malengedwe anawapanga mwamuna ndi mkazi.
7 Cifukwa cace mwamuna adzasiya atate wace ndi amai wace, ndipo adzaphatikizana ndi mkazi wace;
8 ndipo awiriwa adzakhala thupi limodzi: kotero kuti salinso awiri, koma thupi limodzi.
9 Cifukwa cace cimene Mulungu anacimanga pamodzi, asacilekanitse munthu.
10 Ndipo m'nyumba ophunzira anamfunsanso za cinthu ici.